Masalmo 37 BL92

Kusangalala kwa ocimwa kudzatha, olungama akhalitsa nathandizidwa ndi Mulungu

Salmo la Davide.

1 Usabvutike mtima cifukwa ca ocita zoipa,Usacite nsanje cifukwa ca ocita cosalungama.

2 Pakuti adzawamweta msanga monga udzu,Ndipo adzafota monga msipu wauwisi.

3 Khulupirira Yehova, ndipo cita cokoma;Khala m'dziko, ndipo tsata coonadi.

4 Udzikondweretsenso mwa Yehova;Ndipo iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

5 Pereka njira yako kwa Yehova; Khulupiriranso Iye, adzacicita.

6 Ndipo adzaonetsa cilungamo cako monga kuunika,Ndi kuweruza kwako monga usana.

7 Khala cete mwa Yehova, numlindirire Iye:Usabvutike mtima cifukwa ca iye wolemerera m'njira yace,Cifukwa ca munthu wakucita ciwembu.

8 Leka kupsa mtima, nutaye mkwiyo:Usabvutike mtima ungacite coipa,

9 Pakuti ocita zoipa adzadulidwa:Koma iwo akuyembekeza Yehova, iwowa adzalandira dziko lapansi.

10 Katsala kanthawi ndipo woipa adzatha psiti:Inde, udzayang'anira mbuto yace, nudzapeza palibe.

11 Koma ofatsa adzalandira dziko lapansi;Nadzakondwera nao mtendere wocuruka.

12 Woipa apangira ciwembu wolungama,Namkukutira mano.

13 Ambuye adzamseka:Popeza apenya kuti tsiku lace likudza.

14 Oipa anasolola lupanga, nakoka uta wao;Alikhe ozunzika ndi aumphawi,Aphe amene ali oongoka m'njira:

15 Lupanga lao lidzalowa m'mtima mwao momwe,Ndipo mauta ao adzatyoledwa.

16 Zocepa zace za wolungama zikomaKoposa kucuruka kwao kwa oipa ambiri.

17 Pakuti manja a oipa adzatyoledwa:Koma Yehova acirikiza olungama.

18 Yehova adziwa masiku a anthu angwiro:Ndipo cosiyira cao cidzakhala cosatha.

19 Sadzacita manyazi m'nyengo yoipa:Ndipo m'masiku a njala adzakhuta.

20 Pakuti oipa adzatayika,Ndipo adani ace a Yehova adzanga mafuta a ana a nkhosa:Adzanyeka, monga utsi adzakanganuka.

21 Woipa akongola, wosabweza:Koma wolungama acitira cifundo, napereka.

22 Pakuti iwo amene awadalitsa adzalandira dziko lapansi;Koma iwo amene awatemberera adzadulidwa.

23 Yehova akhazikitsa mayendedwe a munthu;Ndipo akondwera nayo njira yace.

24 Angakhale akagwa, satayikiratu:Pakuti Yehova agwira dzanja lace.

25 Ndinali mwana ndipo ndakalamba:Ndipo sindinapenya wolungama wasiyidwa,Kapena mbumba zace zirinkupempha cakudya.

26 Tsiku lonse acitira cifundo, nakongoletsa;Ndipo mbumba zace zidalitsidwa.

27 Siyana naco coipa, nucite cokoma,Nukhale nthawi zonse.

28 Pakuti Yehova akonda ciweruzo,Ndipo sataya okondedwa ace:Asungika kosatha:Koma adzadula mbumba za oipa.

29 Olungama adzalandira dziko lapansi,Nadzakhala momwemo kosatha.

30 Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru,Ndi lilime lace linena ciweruzo.

31 Malamulo a Mulungu wace ali mumtima mwace;Pakuyenda pace sadzaterereka.

32 Woipa aunguza wolungama,Nafuna kumupha.

33 Yehova sadzamsiya m'dzanja lace:Ndipo sadzamtsutsa poweruzidwa iye.

34 Yembekeza Yehova, nusunge njira yace,Ndipo Iye adzakukweza kuti ulandire dziko:Pakudutidwa oipa udzapenya,

35 Ndapenya woipa, alikuopsa,Natasa monga mtengo wauwisi wanzika.

36 Koma anapita ndipo taona, kwati zi:Ndipo ndinampwaira osampeza.

37 Tapenya wangwiro, ndipo taona woongoka mtima!Pakuti ku matsiriziro ace a munthuyo kuti mtendere.

38 Koma olakwa adzaonongeka pamodzi:Matsiriziro a oipa adzadutidwa.

39 Koma cipulumutso ca olungama cidzera kwa Yehova,Iye ndiye mphamvu yao m'nyengo ya nsautso.

40 Ndipo Yehova awathandiza, nawalanditsa:Awalanditsa kwa oipa nawapulumutsa,Cifukwa kuti anamkhulupirira Iye,