Masalmo 107 BL92

Olanditsidwa, alendo, omangidwa, odwala, amarinyero ndi onse ena alemekeze Yehova

1 Yamikani Yehova pakuti Iye ndiye wabwino;Pakuti cifundo cace ncosatha.

2 Atere oomboledwa a Yehova,Amene anawaombola m'dzanja la wosautsa;

3 Nawasokolotsa kumaiko,Kucokera kum'mawa ndi kumadzulo,Kumpoto ndi kunyanja.

4 Anasokera m'cipululu, m'njira yopanda anthu;Osapeza mudzi wokhalamo.

5 Anamva njala ndi ludzu,Moyo wao unakomoka m'kati mwao.

6 Pamenepo anapfuulira kwa Yehova mumsauko mwao,Ndipo anawalanditsa m'kupsinjika kwao.

7 Ndipo anawatsogolera pa njira yolunjika,Kuti amuke ku mudzi wokhalamo.

8 Ayamike Yehova cifukwa ca cifundo cace,Ndi zodabwiza zace za kwa ana a anthu!

9 Pakuti akhutitsa mtima wolakalaka,Nadzaza mtima wanjala ndi zabwino.

10 Iwo akukhala mumdima ndi mu mthunzi wa imfa,Omangika ndi kuzunzika ndi citsulo;

11 Popeza anapikisana nao mau a Mulungu,Napeputsa uphungu wa Wam'mwambamwamba;

12 Kotero kuti anagonjetsa mtima wao ndi cobvuta;Iwowa anakhumudwa koma panalibe mthandizi.

13 Pamenepo anapfuulira kwa Yehova mumsauko mwao,Ndipo anawapulumutsa m'kupsinjika kwao.

14 Anawaturutsa mumdima ndi mu mthunzi wa imfa,Nadula zomangira zao.

15 Ayamike Yehova cifukwa ca cifundo cace,Ndi zodabwiza zace za kwa ana a anthu!

16 Popeza adaswa zitseko zamkuwa,Natyola mipiringidzo yacitsulo.

17 Anthu opusa azunzika cifukwa ca zolakwa zao,Ndi cifukwa ca mphulupulu zao.

18 Mtima wao unyansidwa naco cakudya ciri conse;Ndipo ayandikira zipata za imfa.

19 Pamenepo apfuulira kwa Yehova m'kusauka kwao,Ndipo awapulumutsa m'kupsinjika kwao.

20 Atumiza mau ace nawaciritsa,Nawapulumutsa ku cionongeko cao.

21 Ayamike Yehova cifukwa ca cifundo cace,Ndi zodabwiza zace za kwa ana a anthu!

22 Ndipo apereke nsembe zaciyamiko,Nafotokozere nchito zace ndi kupfuula mokondwera.

23 Iwo akutsikira kunyanja nalowa m'zombo,Akucita nchito zao pa madzi akuru;

24 Iwowa apenya nchito za Yehova,Ndi zodabwiza zace m'madzi ozama.

25 Popeza anena, nautsa namondwe,Amene autsa mafunde ace.

26 Akwera kuthambo, atsikira kozama;Mtima wao usungunuka naco coipaco.

27 Adzandira napambanitsa miyendo ngati munthu woledzeta,Nathedwa nzeru konse.

28 Pamenepo apfuulira kwa Yehova m'kusauka kwao,Ndipo awaturutsa m'kupsinjika kwao.

29 Asanduliza namondwe akhale bata,Kotero kuti mafunde ace atonthole.

30 Pamenepo akondwera, popeza pagwabata;Ndipo Iye awatsogolera kudooko afumko.

31 Ayamike Yehova cifukwa ca cifundo cace,Ndi zodabwiza zace za kwa ana a anthu!

32 Amkwezenso mu msonkhano wa anthu,Namlemekeze pokhala akulu.

33 Asanduliza mitsinje ikhale cipululu,Ndi akasupe a madzi akhale nthaka youma;

34 Dziko lazipatso, likhale lakhulo,Cifukwa ca coipa ca iwo okhalamo.

35 Asanduliza cipululu cikhale tha wale,Ndi dziko louma likhale akasupe a madzi.

36 Ndi apo akhalitsa anjala,Kuti amangeko mudzi wokhalamo anthu;

37 Nafese m'minda, naoke mipesa,Ndiyo vakubata zipatso zolemeza.

38 Ndipo awadalitsa, kotero kuti, acuruka kwambiri;Osacepsanso zoweta zao.

39 Koma acepanso, nawerama,Cifukwa ca cisautso, coipa ndi cisoni.

40 Atsanulira cimpepulo pa akulu,Nawasokeretsa m'cipululu mopanda njira.

41 Koma aika waumphawi pamsanje posazunzika,Nampatsa mabanja ngati gulu la nkhosa.

42 Oongoka mtima adzaciona nadzasekera;Koma cosalungama conse citseka pakamwa pace.

43 Wokhala nazo nzeru asamalire izi,Ndipo azindikire zacifundo za Yehova,