Masalmo 35 BL92

Davide apempha Mulungu alange otpa

Salmo la Davide,

1 Tsutsanani nao iwo akutsutsana nane, Yehova:Limbanani nao iwo akulimbana nane.

2 Gwirani cikopa cocinjiriza, Ukani kundithandiza.

3 Sololani nthungo, ndipo muwatsekerezere kunjira akundilondola:Nenani ndi moyo wanga, Cipulumutso cako ndine.

4 Athe nzeru nacite manyazi iwo akufuna moyo wanga:Abwezedwe m'mbuyo nasokonezeke iwo akundipangira ciwembu.

5 Akhale monga mungu kumphepo,Ndipo mngelo wa Yehova awapitikitse.

6 Njira yao ikhale ya mdima ndi yoterera,Ndipo mngelo wa Yehova awalondole.

7 Pakuti anandichera ukonde wao m'mbunamo kopanda cifukwa,Anakumbira moyo wanga dzenje kopanda cifukwa.

8 Cimgwere modzidzimutsa cionongeko;Ndipo ukonde wace umene anaucha umkole yekha mwini:Agwemo, naonongeke m'mwemo.

9 Ndipo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova:Udzasekera mwa cipulumutso cace.

10 Mafupa anga onse adzanena, Yehova, afanana ndi Inu ndani,Wakulanditsa wozunzika kwa iye amene amposa mphamvu,Ndi wozunzika ndi waumphawi kwa iye amfunkhira?

11 Mboni za ciwawa ziuka,Zindifunsa zosadziwa ine.

12 Andibwezera coipa m'malo mwa cokoma,Inde, asaukitsa moyo wanga.

13 Koma ine, pakudwala iwowa, cobvala canga ndi ciguduli:Ndinazunza moyo wanga ndi kusala;Ndipo pemphero langa linabwera ku cifuwa canga.

14 Ndakhala ine monga ngad iye anali bwenzi langa, kapena mbale wanga:Polira ndinaweramira pansi, monga munthu wakulira maliro amai wace.

15 Ndipo pakutsimphina ine anakondwera, nasonkhana pamodzi:Akundipanda anandisonkhanira; ndipo sindinacidziwa:Ananding'amba osaleka:

16 Pakati pa onyodola pamadyerero,Anandikukutira mano.

17 Ambuye, mudzapenyerabe nthawi yanji?Bwezani moyo wanga kwa zakundiononga zao,Wanga wa wokha kwa misona ya mkango.

18 Ndidzakuyamikanimumsonkhano waukuru:M'cikhamu ca anthu ndidzakulemekezani.

19 Adani anga asandikondwerere ine monyenga;Okwiya nane kopanda cifukwa asanditsinzinire.

20 Pakuti salankhula zamtendere:Koma apangira ciwembu odekha m'dziko.

21 Ndipo andiyasamira m'kamwa mwao;Nati, Hede, Hede, diso lathu lidacipenya.

22 Yehova, mudacipenya; musakhale cete:Ambuye, musakhale kutali ndi ine.

23 Galamukani, ndipo khalani maso kundiweruzira mlandu wanga,Mulungu wanga ndi Ambuye wanga,

24 Mundiweruze monga mwa cilungamo canu, Yehova Mulungu wanga;Ndipo asandisekerere ine.

25 Asanene mumtima mwao, Hede, momwemo!Asanene, Tammeza iye.

26 Acite manyazi, nadodome iwo akukondwera cifukwa ca coipa cidandigwera:Abvekeke ndi manyazi ndi kupunzika iwo akudzikuza pa ine.

27 Apfuule mokondwera nasangalale iwo akukondwera naco cilungamo canga:Ndipo anene kosalekeza, Abuke Yehova,Amene akondwera ndi mtendere wa mtumiki wace.

28 Ndipo lilime langa lilalikire cilungamo canu,Ndi lemekezo lanu tsiku lonse.