Masalmo 59 BL92

Davide apempha Mulungu amlanditse, nadzinenera wosalakwa

Kwa Mkulu wa Nyimbo; pa Altasbeti. Mikta mu wa Davide. Muja anatuma adikire nyumba yace, kuti amuphe,

1 Ndilanditseni kwa adani anga, Mulungu wanga:Ndiikeni pamsanje kwa iwo akundiukira.

2 Mundilanditse kwa ocita zopanda pace,Ndipo ndipulumutseni kwa anthu olira mwazi.

3 Pakuti onani, alalira moyo wanga;Amphamvu andipangira ciwembu:Osacimwa, osalakwa ine, Yehova,

4 Osawapatsa cifukwa ine, athamanga nadzikonza;Galamukani kukomana nane, ndipo penyani.

5 Ndinu Yehova, Mulungu wa makamu, Mulungu wa Israyeli,Ukani kukazonda amitundu onse:Musacitire cifundo mmodzi yense wakucita zopanda pace monyenga.

6 Abwera madzulo, auwa ngati garu,Nazungulira mudzi.

7 Onani abwetuka pakamwa pao;M'milomo mwao muli lupanga,Pakuti amati, Amva ndani?

8 Koma Inu, Yehova, mudzawaseka;Mudzalalatira amitundu onse.

9 Inu, mphamvu yanga, ndidzakulindirani;Pakuti Mulungu ndiye msanje wanga.

10 Mulungu wa cifundo canga adzandikumika:Adzandionetsa tsoka la adani anga.

11 Musawapheretu, angaiwale anthu anga:Muwabalalitse mwa mphamvu yanu, ndipo muwagwetse,Ambuye, ndinu cikopa cathu.

12 Pakamwa pao acimwa ndi mau onse a pa milomo yao,Potero akodwe m'kudzitamandira kwao,Ndiponso cifukwa ca kutemberera ndi bodza azilankhula.

13 Muwathe mumkwiyo, muwagurule psiti:Ndipo adziwe kuti Mulungu ndiye woweruza m'Yakobo,Kufikira malekezero a dziko la pansi.

14 Ndipo abwere madzulo, auwe ngati garu,Nazungulire mudzi.

15 Ayendeyende ndi kufuna cakudya,Nacezere osakhuta.

16 Koma ine, ndidzayimbira mphamvu yanu;Inde ndidzayimbitsa cifundo canu mamawa:Pakuti Inu mwakhala msanje wanga,Ndi pothawirapo ine tsiku la nsautso yanga.

17 Ndidzayimbira zakukulemekezani Inu, mphamvu yanga:Pakuti Mulungu ndiye msanje wanga, Mulungu wa cifundo canga.