Masalmo 44 BL92

Anthu a Mulungu akumbuke zithandizo zakale popempha cipulumutso m'tsoka lao

Kwa Mkulu Wa Nyimbo; Cuangizo ca ana a Kora.

1 Mulungu, tidamva m'makutu mwathu, makolo athu anatisimbira,Za nchitoyo mudaicita masiku ao, masiku akale.

2 Inu munapitikitsa amitundu ndi dzanja lanu, koma iwowa munawaoka;Munasautsa mitundu ya anthu, ndipo munawaingitsa,

3 Pakuti sanalanda dziko ndi lupanga lao,Ndipo mkono wao sunawapulumutsa:Koma dzanja lanu lamanja, ndi mkono wanu, ndi kuunika kwa nkhope yanu.Popeza munakondwera nao,

4 Inu ndinu mfumu yanga, Mulungu:Lamulirani cipulumutso ca Yakobo.

5 Mwa Inu tidzakankhira pansi otsutsana nafe:M'dzina lanu tidzapondereza akutiukira ife.

6 Pakuti sinditama uta wanga,Ndipo lupanga langa silingandipulumutse.

7 Koma Inu munatipulumutsa kwa iwo akutsutsana nafe,Ndipo akudana nafe, mudawacititsa manyazi.

8 Mwa Mulungu tidzitamanda tsiku lonse,Ndipo dzina lanu tidzaliyamika kosatha.

9 Koma mwatitaya, ndi kutinyazitsa;Ndipo simuturuka nao makamu a nkhondo athu.

10 Mutibwereretsa kuthawa otisautsa:Ndipo akudana nafe adzifunkhira okha.

11 Mwatipereka ngati nkhosa zoyenera kuzidya;Ndipo mwatibalalitsa mwa amitundu.

12 Mugulitsa anthu anu kwacabe,Ndipo mtengo wace simupindula nao.

13 Mutisandutsa cotonza kwa anzathu,Ndi coseketsa ndi colalatitsa iwo akutizinga.

14 Mutiika tikhale onyozeka mwa amitundu,Ndi kuti anthu atipukusire mitu.

15 Tsiku lonse cimpepulo canga cikhala pamaso panga,Ndipo manyazi a pankhope panga andikuta.

16 Cifukwa ca mau a wotonza wocitira mwano;Cifukwa ca mdani ndi wobwezera cilango,

17 Zonsezi zatigwera; koma sitinakuiwalani,Ndipo sitinacita monyenga m'pangano lanu.

18 Mtima wathu sunabwerera m'mbuyo,Ndipo m'mayendedwe athu sitinapatuka m'njira yanu;

19 Mungakhale munatityola mokhala zirombo,Ndi kutiphimba nao mthunzi wa imfa.

20 Tikadaiwala dzina la Mulungu wathu,Ndi kutambasulira manja athu kwa mulungu wacilendo;

21 Mulungu sakadasanthula ici kodi?Pakuti adziwa zinsinsi za mtima.

22 Koma, cifukwa ca Inu, tiphedwa tsiku lonse;Tiyesedwa ngati nkhosa zakuzipha.

23 Galamukani, mugoneranji, Ambuye?Ukani, musatitaye citayire.

24 Mubisiranji nkhope yanu,Ndi kuiwala kuzunzika ndi kupsinjika kwathu?

25 Pakuti moyo wathu waweramira kupfumbi:Pamimba pathu pakangamira dziko lapansi.

26 Ukani, tithandizeni,Tiomboleni mwa cifundo canu.