Masalmo 119 BL92

Cilamulo ca Mulungu ndi cokometsetsa. Adalitsidwa akucisunga

1 Odala angwiro m'mayendedwe ao,Akuyenda m'cilamulo ca Yehova.

2 Odala iwo akusunga mboni zace,Akumfuna ndi mtima wonse;

3 Inde, sacita cosalungama;Ayenda m'njira zace.

4 Inu munatilamulira.Tisamalire malangizo anu ndi cangu,

5 Ha! mwenzi zitakhazikika njira zangaKuti ndisamalire malemba anu.

6 Pamenepo sindidzacita manyazi,Pakupenyerera malamulo anu onse.

7 Ndidzakuyanrikani ndi mtima woongoka,Pakuphunzira maweruzo anu olungama.

8 Ndidzasamalira malemba anu:Musandisiye ndithu.

9 Mnyamata adzayeretsa mayendedwe ace bwanji?Akawasamalira monga mwa mau anu.

10 Ndinakufunani ndi mtima wanga wonse;Ndisasokere kusiyana nao malamulo anu.

11 Ndinawabisa mau anu mumtima mwanga,Kuti ndisalakwire Inu.

12 Inu ndinu wodala Yehova;Ndiphunzitseni malemba anu.

13 Ndinafotokozera ndi milomo yangaMaweruzo onse a pakamwa panu,

14 Ndinakondwera m'njira ya mboni zanu,Koposa ndi cuma conse,

15 Ndidzalingirira pa malangizo anu,Ndi kupenyerera mayendedwe anu.

16 Ndidzadzikondweretsa nao malemba anu;Sindidzaiwala mau anu,

17 Mucitire cokoma mtumiki wanu kuti ndikhale ndi moyo;Ndipo ndidzasamalira mau anu.

18 Munditsegulire maso, kuti ndipenyeZodabwiza za m'cilamulo canu.

19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi;Musandibisire malamulo anu.

20 Mtima wanga wasweka ndi kukhumbaMaweruzo anu nyengo zonse.

21 Munadzudzula odzikuza otembereredwa,Iwo akusokera kusiyana nao malamulo anu.

22 Mundicotsere cotonza, ndi cimpepulo;Pakuti ndinasunga mboni zanu.

23 Nduna zomwe zinakhala zondineneza;Koma mtumiki wanu analingirira malemba anu.

24 Mboni zanu zomwe ndizo zondikondwetsa,Ndizo zondipangira nzeru.

25 Moyo wanga umamatika ndi pfumbi;Mundipatse moyo monga mwa mau anu.

26 Ndinafotokozera njira zanga, ndipo munandiyankha:Mundiphunzitse malemba anu.

27 Mundizindikiritse njira ya malangizo anu;Kuti ndilingalire zodabwiza zanu.

28 Moyo wanga wasungunuka ndi cisoni:Mundilimbitse monga mwa mau anu.

29 Mundicotsere njira ya cinyengo;Nimundipatse mwacifundo cilamulo canu.

30 Ndinasankha njira yokhulupirika;Ndinaika maweruzo anu pamaso, panga,

31 Ndimamatika nazo mboni zanu;Musandicititse manyazi, Yehova.

32 Ndidzathamangira njira ya malamulo anu,Mutakulitsa mtima wanga.

33 Mundiphunzitse, Yehova, njira ya malemba anu;Ndidzaisunga kufikira kutha kwace.

34 Mundizindikiritse, ndipo ndidzasunga malamulo anu;Ndidzawasamalira ndi mtima wanga wonse.

35 Mundiyendetse mopita malamulo anu;Pakuti ndikondwera m'menemo.

36 Lingitsani mtima wanga ku mboni zanu,Si ku cisiriro ai.

37 Mucititse mlubza maso anga ndisapenye zacabe,Mundipatse moyo mu njira yanu.

38 Limbitsirani mtumiki wanu mau anu,Ndiye wodzipereka kukuopani.

39 Mundipatutsire cotonza canga ndiciopaco;Popeza maweruzo anu ndi okoma.

40 Taonani, ndinalira malangizo anu;Mundipatse moyo mwa cilungamo canu.

41 Ndipo cifundo canu cindidzere, Yehova,Ndi cipulumutso canu, monga mwa mau anu.

42 Kuti ndikhale nao mau akuyankha wonditonza;Popeza ndikhulupirira mau anu.

43 Ndipo musandicotsere ndithu mau a coonadi pakamwa panga;Pakuti ndinayembekeza maweruzo anu.

44 Potero ndidzasamalira malamulo anu cisamalireKu nthawi za nthawi.

45 Ndipo ndidzayenda mwaufulu;Popeza ndinafuna malangizo anu.

46 Ndidzalankhulanso za umboni wanu pamaso pa mafumu,Osacitapo manyazi.

47 Ndipo ndidzadzikondweretsa nao malamulo anu,Amene ndiwakonda.

48 Ndidzakwezanso manja anga ku malamulo anu, amene ndiwakonda;Ndipo ndidzalingalira pa malemba anu.

49 Kumbukilani mau a kwa mtumiki wanu,Amene munandiyembekezetsa nao.

50 Citonthozo canga m'kuzunzika kwanga ndi ici;Pakuti mau anu anandipatsa moyo.

51 Odzikuza anandinyoza kwambiri:Koma sindinapatukanso naco cilamulo canu.

52 Ndinakumbukila maweruzo anu kuyambira kale, Yehova,Ndipo ndinadzitonthoza.

53 Ndinasumwa kwakukuru,Cifukwa ca oipa akusiya cilamulo canu.

54 Malemba anu anakhala nyimbo zangaM'nyumba ya ulendo wanga,

55 Usiku ndinakumbukila dzina lanu, Yehova,Ndipo ndinasamalira cilamulo canu.

56 Ici ndinali naco,Popeza ndinasunga malangizo anu.

57 Yehova ndiye gawo langa:Ndinati ndidzasunga mau anu.

58 Ndinapemba pankhope panu ndi mtima wanga wonse:Mundicitire cifundo monga mwa mau anu.

59 Ndinaganizira njira zanga,Ndipo ndinabweza mapazi anga atsate mboni zanu.

60 Ndinafulumira, osacedwa,Kusamalira malamulo anu.

61 Anandikulunga nazo zingwe za oipa;Koma sindinaiwala cilamulo canu.

62 Pakati pa usiku ndidzauka kukuyamikaniCifukwa ca maweruzo anu olungama.

63 Ine ndine wakuyanjana nao onse akukuopani,Ndi iwo akusamalira malangizo anu.

64 Dziko lapansi lidzala naco cifundo canu, Yehova;Mundiphunzitse malemba anu.

65 Munacitira mtumiki wanu cokoma, Yehova,Monga mwa mau anu.

66 Mundiphunzitse cisiyanitso ndi nzeru;Pakuti ndinakhulupirira malamulo anu.

67 Ndisanazunzidwe ndinasokera; Koma tsopano ndisamalira mau anu.

68 Inu ndinu wabwino, ndi wakucita zabwino;Mundiphunzitse malemba anu.

69 Odzikuza anandipangira bodza:Ndidzasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.

70 Mtima wao unona ngati mafuta;Koma ine ndikondwera naco cilamulo canu.

71 Kundikomera kuti ndinazunzidwa;Kuti ndiphunzire malemba anu.

72 Cilamulo ca pakamwa panu cindikomeraKoposa golidi ndi siliva zikwi zikwi.

73 Manja anu anandilenga nandiumba;Mundizindikiritse, kuti ndiphunzire malemba anu.

74 Iwo amene akuopani adzandiona ine nadzakondwera;Popeza ndayembekezera mau anu;

75 Ndidziwa kuti maweruzo anu ndiwo olungama, Yehova,Ndi kuti munandizunza ine mokhulupirika.

76 Cifundo canu cikhaletu cakunditonthoza, ndikupemphani,Monga mwa mau anu kwa mtumiki wanu.

77 Nsoni zokoma zanu zindidzere, kuti ndikhale ndi moyo;Popeza cilamulo canu cindikondweretsa.

78 Odzikuza acite manyazi, popeza anandicitira monyenga ndi bodza:Koma ine ndidzalingalira malangizo anu.

79 Iwo akuopa Inu abwere kwa ine,Ndipo adzadziwa mboni zanu.

80 Mtima wanga ukhale wangwiro m'malemba anu;Kuti ndisacite manyazi.

81 Moyo wanga unakomoka ndi kukhumba cipulumutso canu:Ndinayembekezera mau anu.

82 Maso anga anatha mphamvu ndi kukhumba mau anu,Ndikuti, Mudzanditonthoza liti?

83 Popeza ndakhala ngati thumba lofukirira;Koma sindiiwala malemba anu.

84 Masiku a mtumiki wanu ndiwo angati?Mudzaweruza liti iwo akundilondola koipa?

85 Odzikuza anandikumbira mbuna,Ndiwo osasamalira cilamulo canu.

86 Malamulo anu onse ngokhulupirika;Andilondola nalo bodza; ndithandizeni.

87 Akadandithera pa dziko lapansi; Koma ine sindinasiya malangizo anu.

88 Mundipatse moyo monga mwa cifundo canu;Ndipo ndidzasamalira mboni ya pakamwa panu,

89 Mau anu aikika kumwamba,Kosatha, Yehova.

90 Cikhulupiriko canu cifikira mibadwo mibadwo;Munakhazikitsa dziko lapansi, ndipo likhalitsa.

91 Kunena za maweruzo anu alimbikira kufikira lero;Pakuti onsewa ndiwo atumiki anu.

92 Cilamulo canu cikadapanda kukhala cikondweretso canga,Ndikadatayika m'kuzunzika kwanga.

93 Sindidzaiwala malangizo anu nthawi zonse;Popeza munandipatsa nao moyo.

94 Ine ndine wanu, ndipulumutseniPakuti ndinafuna malangizo anu.

95 Oipa anandilalira kundiononga;Koma ndizindikira mboni zanu.

96 Ndinapenya malekezero ace a ungwiro wonse;Koma lamulo lanu ndi lotakasuka ndithu.

97 Ha! Ndikondadi cilamulo canu;Ndilingiriramo ine tsiku lonse.

98 Malamulo anu andipatsa nzeru yakuposa adani anga;Pakuti akhala nane cikhalire.

99 Ndiri nayo nzeru yakuposa aphunzitsi anga onse;Pakuti ndilingalira mboni zanu.

100 Ndizindikira koposa okalambaPopeza ndinasunga malangizo anu.

101 Ndinaletsa mapazi anga njira iri yonse yoipa,Kuti ndisamalire mau anu.

102 Sindinapatukana nao maweruzo anu;Pakuti Inu munandiphunzitsa.

103 Mau anu azunadi powalawa ine!Koposa uci m'kamwa mwanga.

104 Malangizo anu andizindikiritsa;Cifukwa cace ndidana nao mayendedwe onse acinyengo,

105 Mau anu ndiwo nyali ya ku mapazi anga,Ndi kuunika kwa panjira panga,

106 Ndinalumbira, ndipo ndinatsimikiza mtima,Kuti ndidzasamalira maweruzo anu olungama.

107 Ndazunzika kwambiri:Ndipatseni moyo, Yehova, monga mwa mau anu.

108 Landirani, Yehova, zopereka zaufulu za pakamwa panga,Ndipo ndiphunzitseni maweruzo anu.

109 Moyo wanga ukhala m'dzanja langa cikhalire;Koma sindiiwala cilamulo canu.

110 Oipa anandichera msampha;Koma sindinasokera m'malangizo anu.

111 Ndinalandira mboni zanu zikhale colandira cosatha;Pakuti ndizo zokondweretsa mtima wanga.

112 Ndinalingitsa mtima wanga ucite malemba anu,Kosatha, kufikira cimatiziro.

113 Ndidana nao a mitima iwiri;Koma ndikonda cilamulo canu.

114 Inu ndinu pobisalapo panga, ndi cikopa canga;Ndiyembekezera mau anu.

115 Mundicokere ocita zoipa inu;Kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga.

116 Mundicirikize monga mwa mau anu, kuti ndikhale ndi moyo;Ndipo ndisacite manyazi pa ciyembekezo canga.

117 Mundigwirizize ndipo ndidzapulumutsidwa,Ndipo ndidzasamalira malemba anu cisamalire.

118 Mupepulaonseakusokeram'malemba anu;Popeza cinyengo cao ndi bodza.

119 Mucotsa oipa onse a pa dziko lapansi ngati mphala:Cifukwa cace ndikonda mboni zanu.

120 Thupi langa linjenjemera ndi kuopa Inu;Ndipo ndicita mantha nao maweruzo anu.

121 Ndinacita ciweruzo ndi cilungamo;Musandisiyira akundisautsa.

122 Mumkhalire cikole mtumiki wanucimkomere;Odzikuza asandisautse.

123 Maso anga anatha mphamvu pafuna cipulumutso canu,Ndi mau a cilungamo canu.

124 Mucitire mtumiki wanu monga mwa cifundo canu,Ndipo ndiphunzitseni malemba anu,

125 Ine ndine mtumiki wanu, ndizindikiritseni;Kuti ndidziwe mboni zanu.

126 Yafika nyengo yakuti Yehova acite kanthu;Pakuti anaswa cilamulo canu.

127 Cifukwa cace ndikonda malamulo anuKoposa golidi, Inde golidi woyengeka,

128 Cifukwa cace ndiyesa ngolunjika malangizo anu onse akunena zonse;Koma ndidana nazo njira zonse zonyenga.

129 Mboni zanu nzodabwiza; Cifukwa cace moyo wanga uzisunga,

130 Potsegulira mau anu paunikira;Kuzindikiritsa opusa.

131 Ndinatsegula pakamwa panga, ndi kupuma wefu wefu;Popeza ndinakhumba malamulo anu.

132 Munditembenukire, ndi kundicitira cifundo,Monga mumatero nao akukonda dzina lanu.

133 Kfiazikitsanimapaziangam'mau anu;Ndipo zisandigonjetse zopanda pace ziri zonse.

134 Mundiombole ku nsautso ya munthu:Ndipo ndidzasamalira malangizo anu.

135 Muwalitse nkhope yanu pa mtumiki wanu;Ndipo mundiphunzitse malemba anu.

136 Maso anga atsitsa mitsinje ya madzi,Popeza sasamalira cilamulo canu.

137 Inu ndinu wolungama, Yehova,Ndipo maweruzo anu ndiwo olunjika.

138 Mboni zanuzo mudazilamuliraZiri zolungama ndi zokhulupirika ndithu.

139 Cangu canga cinandithera,Popeza akundisautsa anaiwala mau anu.

140 Mau anu ngoyera ndithu;Ndi mtumiki wanu awakonda.

141 Wamng'ono ine, ndi wopepulidwa;Koma sindiiwala malemba anu.

142 Cilungamo canu ndico cilungamo cosatha;Ndi cilamulo canu ndico coonadi.

143 Kusautsika ndi kupsinjika kwandigwera;Koma malamulo anu ndiwo ondikondweretsa ine.

144 Mboni zanu ndizo zolungama kosatha;Mundizindikiritse izi, ndipo ndidzakhala ndi moyo.

145 Ndinaitana ndi mtima wanga wonse; mundiyankhe, Yehova;Ndidzasunga malemba anu.

146 Ndinaitanira Inu; ndipulumutseni,Ndipo ndidzasamalira mboni zanu.

147 Ndinapfuula kusanace:Ndinayembekezera mau anu.

148 Maso anga anakumika malonda a usiku,Kuti ndilingirire mau anu.

149 Imvani liu langa monga mwa cifundo canu;Mundipatse moyo monga mwa kuweruza kwanu, Yehova.

150 Otsata zaciwembu andiyandikira;Akhala kutali ndi cilamulo canu.

151 Inu muli pafupi, Yehova;Ndipo malamulo anu onse ndiwo coonadi,

152 Kuyambira kale ndinadziwa mu mboni zanu,Kuti munazikhazika kosatha,

153 Penyani kuzunzika kwanga, nimundilanditse;Pakuti sindiiwala cilamulo canu.

154 Mundinenere mlandu wanga, nimundiombole;Mundipatse moyo monga mwa mau anu.

155 Cipulumutso citalikira oipa;Popeza safuna malemba anu.

156 Zacifundo zanu ndi zazikuru, Yehova;Mundipatse moyo monga mwa maweruzo anu.

157 Ondilondola ndi ondisautsa ndiwoambiri;Koma sindinapatukana nazo mboni zanu.

158 Ndinapenya ocita monyenga, ndipo ndinanyansidwa nao;Popeza sasamalira mau anu.

159 Penyani kuti ndikonda malangizo anu;Mundipatse moyo, Yehova, monga mwa cifundo canu.

160 Ciwerengero ca mau anu ndico coonadi;Ndi maweruzo anu olungama onse akhala kosatha.

161 Nduna zinandilondola kopanda cifukwa;Koma mtima wanga ucita mantha nao mau anu.

162 Ndikondwera nao mau anu,Ngati munthu wakupeza zofunkha zambiri.

163 Ndidana nalo bodza ndi kunyansidwa nalo;Koma ndikonda cilamulo canu.

164 Ndikulemekezani kasanu ndi kawiri, tsiku limodzi,Cifukwa ca maweruzo anu alungama.

165 Akukonda cilamulo canu ali nao mtendere wambiri;Ndipo alibe cokhumudwitsa.

166 Ndinayembekeza cipulumutso canu, Yehova,Ndipo ndinacita malamulo anu.

167 Moyo wanga unasamalira mboni zanu;Ndipo ndizikonda kwambiri.

168 Ndinasamalira malangizo anu ndi mboni zanu;Popeza njira zanga zonse ziri pamaso panu,

169 Kupfuula kwanga kuyandikire pamaso pano, Yehova;Mundizindikiritse monga mwa mau anu.

170 Kupemba kwanga kudze pamaso panu;Mundilanditse monga mwa mau anu.

171 Milomo yanga iturutse cilemekezo;Popeza mundiphunzitsa malemba anu.

172 Lilime langa liyimbire mau anu;Pakuti malamulo anu onse ndiwo olungama.

173 Dzanja lanu likhale lakundithandizaPopezandinasankha malangizo anu.

174 Ndinakhumba cipulumutso canu, Yehova;Ndipo cilamulo canu ndico condikondweretsa.

175 Mzimu wanga ukhale ndi moyo, ndipo udzakulemekezani;Ndipo maweruzo anu andithandize.

176 Ndinasocera ngati nkhosa yotayika; funani mtumiki wanu;Pakuti sindiiwala malamulo anu.