7 M'kamwa mwace mwadzala kutemberera ndi manyengo ndi kucenjerera;Pansi pa lilime lace pali cibvutitso copanda pace.
8 Akhala m'molalira midzi;Mobisalamo akupha munthu wosacimwa:Ambisira waumphawi nkhope yace,
9 Alalira monga mkango m'ngaka mwace;Alalira kugwira wozunzika:Agwira wozunzika, pakumkola m'ukonde mwace.
10 Aunthama, nawerama,Ndipo aumphawi agwa m'zala zace.
11 Anena m'mtima mwace, Mulungu waiwala;Wabisa nkhope yace; sapenya nthawi zonse,
12 Ukani, Yehova; samulani dzanja lanu, Mulungu;Musaiwale ozunzika.
13 Woipa anyozeranii Mulungu,Anena m'mtima mwace, Simudzafunsira?