23 Iye analanda mphamvu yanga panjira;Anacepsa masiku anga.
24 Ndinati, Mulungu wanga, musandicotse pakati pa masiku anga:Zaka zanu zikhalira m'mibadwo mibadwo.
25 Munakhazika dziko lapansi kalelo;Ndipo zakumwamba ndizo nchito ya manja anu.
26 Zidzatha izi, koma Inu mukhala:Inde, zidzatha zonse ngati cabvala;Mudzazisintha ngati maraya, ndipo zidzasinthika:
27 Koma Inu ndinu yemweyo,Ndi zaka zanu sizifikira kutha.
28 Ana a atumiki anu adzakhalitsa,Ndi mbeu zao zidzakhazikika pamaso panu.