25 Munakhazika dziko lapansi kalelo;Ndipo zakumwamba ndizo nchito ya manja anu.
26 Zidzatha izi, koma Inu mukhala:Inde, zidzatha zonse ngati cabvala;Mudzazisintha ngati maraya, ndipo zidzasinthika:
27 Koma Inu ndinu yemweyo,Ndi zaka zanu sizifikira kutha.
28 Ana a atumiki anu adzakhalitsa,Ndi mbeu zao zidzakhazikika pamaso panu.