4 Mtima wanga ukunga udzu wamweta, nufota;Popeza ndiiwala kudya mkate wanga.
5 Cifukwa ca liu la kubuula kwangaMnofu wanga umamatika ku mafupa anga.
6 Ndikunga bvuwo m'cipululu;Ndikhala ngati kadzidzi wa kumabwinja.
7 Ndidikira, ndikhala ngati mbawaIri yokha pamwamba pa tsindwi.
8 Adani anga anditonza tsiku lonse;Akundiyarukirawo alumbirira ine.
9 Pakuti ndadya mapulusa ngati mkate,Ndi kusanganiza-comwera canga ndi misozi,
10 Cifukwa ca ukali wanu ndi kuzaza kwanu;Popeza munandinyamula ndipo munandigwetsa.