2 Lemekeza Yehova, moyo wanga,Ndi kusaiwala zokoma zace zonse aticitirazi:
3 Amene akhululukira mphulupulu zako zonse;Naciritsa nthenda zako zonse;
4 Amene aombola moyo wako ungaonongeke;Nakubveka korona wa cifundo ndi nsoni zokoma:
5 Amene akhutitsa m'kamwa mwako ndi zabwino;Nabweza ubwana wako unge mphungu.
6 Yehova acitira onse osautsidwa Cilungamo ndi ciweruzo.
7 Analangiza Mose njira zace,Ndi ana a Israyeli macitidwe ace.
8 Yehova ndiye wa nsoni zokoma ndi wacisomo,Wosakwiya msanga, ndi wa cifundo cocuruka.