5 Amene akhutitsa m'kamwa mwako ndi zabwino;Nabweza ubwana wako unge mphungu.
6 Yehova acitira onse osautsidwa Cilungamo ndi ciweruzo.
7 Analangiza Mose njira zace,Ndi ana a Israyeli macitidwe ace.
8 Yehova ndiye wa nsoni zokoma ndi wacisomo,Wosakwiya msanga, ndi wa cifundo cocuruka.
9 Sadzatsutsana nao nthawi zanse;Ndipo sadzasunga mkwiyo wace kosatha.
10 Sanaticitira monga mwa zolakwa zathu,Kapena kutibwezera monga mwa mphulupulu zathu.
11 Pakuti monga m'mwamba mutalikira ndi dziko lapansi,Motero cifundo cace cikulira iwo akumuopa Iye.