5 Anakhazika dziko lapansi pa maziko ace,Silidzagwedezeka ku nthawi yonse.
6 Mudalikuta ndi nyanja ngati ndi cobvala;Madzi anafikira pamwamba pa mapiri,
7 Pa kudzudzula kwanu anathawa;Anathawa msanga liu la bingu lanu;
8 Anakwera m'mapiri, anatsikira m'zigwa,Kufikira malo mudawakonzeratu.
9 Munaika malire kuti asapitirireko;Kuti asabwererenso kuphimba dziko lapansi.
10 Atumiza akasupe alowe m'makwawa;Ayenda pakati pa mapiri:
11 Zimamwamo nyama zonse za kuthengo;Mbidzi zipherako ludzu lao.