1 Yamikani Yehova, itanirani pa dzina lace;Bukitsani mwa mitundu ya anthu zocita Iye.
2 Myimbireni, myimbireni zomlemekeza;Fotokozerani zodabwiza zace zonse.
3 Mudzitamandire ndi dzina lace loyera:Mitima yao ya iwo ofunsira Yehova ikondwere.
4 Funani Yehova, ndi mphamvu yace;Funsirani nkhope yace nthawi zonse.
5 Kumbukilani zodabwiza zace adazicita;Zizindikilo zace ndi maweruzo a pakamwa pace;
6 Inu mbeu za Abrahamu, mtumiki wace,Inu ana a Yakobo, osankhika ace.