11 Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani,Gawo la colandira cako;
12 Pokhala iwo anthu owerengeka,Inde, anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo;
13 Nayendayenda kucokera mtundu wina kufikira mtundu wina,Kucokera ufumu wina kufikira anthu ena.
14 Sanalola munthu awasautse;Ndipo anadzudzula mafumu cifukwa ca iwowa;
15 Ndi kuti musamakhudza odzozedwa anga,Musamacitira coipa aneneri anga.
16 Ndipo anaitana njala igwere dziko;Anatyola mcirikizo wonse wa mkate.
17 Anawatsogozeratu munthu;Anamgulitsa Yosefe akhale kapolo: