13 Nayendayenda kucokera mtundu wina kufikira mtundu wina,Kucokera ufumu wina kufikira anthu ena.
14 Sanalola munthu awasautse;Ndipo anadzudzula mafumu cifukwa ca iwowa;
15 Ndi kuti musamakhudza odzozedwa anga,Musamacitira coipa aneneri anga.
16 Ndipo anaitana njala igwere dziko;Anatyola mcirikizo wonse wa mkate.
17 Anawatsogozeratu munthu;Anamgulitsa Yosefe akhale kapolo:
18 Anapweteka miyendo yace ndi matangadza;Anamgoneka m'unyolo;
19 Kufikira nyengo yakucitika maneno ace;Mau a Yehova anamuyesa.