15 Ndi kuti musamakhudza odzozedwa anga,Musamacitira coipa aneneri anga.
16 Ndipo anaitana njala igwere dziko;Anatyola mcirikizo wonse wa mkate.
17 Anawatsogozeratu munthu;Anamgulitsa Yosefe akhale kapolo:
18 Anapweteka miyendo yace ndi matangadza;Anamgoneka m'unyolo;
19 Kufikira nyengo yakucitika maneno ace;Mau a Yehova anamuyesa.
20 Mfumuyo anatuma munthu nammasula;Woweruza mitundu ya anthu anamtsegulira.
21 Anamuika akhale woyang'anira nyumba yace,Ndi woweruza wa pa zace zonse: