18 Anapweteka miyendo yace ndi matangadza;Anamgoneka m'unyolo;
19 Kufikira nyengo yakucitika maneno ace;Mau a Yehova anamuyesa.
20 Mfumuyo anatuma munthu nammasula;Woweruza mitundu ya anthu anamtsegulira.
21 Anamuika akhale woyang'anira nyumba yace,Ndi woweruza wa pa zace zonse:
22 Amange nduna zace iye mwini,Alangize akulu ace adziwe nzeru.
23 Pamenepo Israyeli analowa m'Aigupto;Ndi Yakobo anakhala mlendo m'dziko la Hamu.
24 Ndipo anacurukitsatu mtundu wa anthu ace,Nawapatsa mphamvu yoposa owasautsa.