23 Pamenepo Israyeli analowa m'Aigupto;Ndi Yakobo anakhala mlendo m'dziko la Hamu.
24 Ndipo anacurukitsatu mtundu wa anthu ace,Nawapatsa mphamvu yoposa owasautsa.
25 Anasanduliza mitima yao, kuti adane nao anthu ace,Kuti acite monyenga ndi atumiki ace.
26 Anatuma Mose mtumiki wace, Ndi Aroni amene adamsankha.
27 Anaika pakati pao zizindikilo zace,Ndi zodabwiza m'dziko la Hamu.
28 Anatumiza mdima ndipo kunada;Ndipo sanapikisana nao mau ace.
29 Anasanduliza madzi ao akhale mwazi,Naphanso nsomba zao.