28 Anatumiza mdima ndipo kunada;Ndipo sanapikisana nao mau ace.
29 Anasanduliza madzi ao akhale mwazi,Naphanso nsomba zao.
30 Dziko lao linacuruka acule,M'zipinda zomwe za mafumu ao.
31 Ananena, ndipo inadza mitambo ya nchenche,Ndi nsabwe kufikira m'malire ao onse.
32 Anawapatsa mvula yamatalala,Lawi la moto m'dziko lao.
33 Ndipo anapanda mipesa yao, ndi mikuyu yao;Natyola mitengo kufikira m'malire ao onse.
34 Ananena, ndipo linadza dzombeNdi mphuci, ndizo zosawerengeka,