36 Ndipo Iye anapha acisamba onse m'dziko mwaoCoyambira ca mphamvu yao yonse.
37 Ndipo anawaturutsa pamodzi ndi siliva ndi golidi:Ndi mwa mafuko ao munalibe mmodzi wokhumudwa.
38 Aigupto anakondwera pakucoka iwo;Popeza kuopsa kwao kudawagwera.
39 Anayala mtambo uwaphimbe;Ndi moto uunikire usiku,
40 Anafunsa ndipo Iye anadzetsa zinziri.Nawakhuritsa mkate wakumwamba.
41 Anatsegula pathanthwe, anaturukamo madzi;Nayenda pouma ngati mtsinje.
42 Popeza anakumbukila mau ace oyera,Ndi Abrahamu mtumiki wace.