38 Aigupto anakondwera pakucoka iwo;Popeza kuopsa kwao kudawagwera.
39 Anayala mtambo uwaphimbe;Ndi moto uunikire usiku,
40 Anafunsa ndipo Iye anadzetsa zinziri.Nawakhuritsa mkate wakumwamba.
41 Anatsegula pathanthwe, anaturukamo madzi;Nayenda pouma ngati mtsinje.
42 Popeza anakumbukila mau ace oyera,Ndi Abrahamu mtumiki wace.
43 Potero anaturutsa anthu ace ndi kusekerera,Osankhika ace ndi kupfuula mokondwera.
44 Ndipo anawapatsa maiko a amitundu;Iwo ndipo analanda zipatso za nchito ya anthu: