8 Akumbukila cipangano cace kosatha,Mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;
9 Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu,Ndi lumbiro lace ndi Isake;
10 Ndipo anaciimikira Yakobo, cikhale malemba,Cikhale cipangano cosatha kwa Israyeli.
11 Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani,Gawo la colandira cako;
12 Pokhala iwo anthu owerengeka,Inde, anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo;
13 Nayendayenda kucokera mtundu wina kufikira mtundu wina,Kucokera ufumu wina kufikira anthu ena.
14 Sanalola munthu awasautse;Ndipo anadzudzula mafumu cifukwa ca iwowa;