13 Koma anaiwala nchito zace msanga;Sanalindira uphungu wace:
14 Popeza analaka-lakatu kucidikhako,Nayesa Mulungu m'cipululu.
15 Ndipo anawapatsa copempha iwo;Koma anaondetsa mitima yao.
16 Ndipo kumisasa anacita nao nsanje MoseNdi Aroni woyerayo wa Yehova.
17 Dziko lidayasama nilidameza Datani,Ndipo linafotsera gulu la Abiramu.
18 Ndipo m'gulu mwao mudayaka moto;Lawi lace lidapsereza oipawo.
19 Anapanga mwana wa ng'ombe ku Horebu,Nagwadira fano loyenga.