22 Zodabwiza m'dziko la Hamu,Zoopsa ku Nyanja Yofiira.
23 Potero Iye adati awaononge,Pakadapanda Mose wosankhika wace, kuima pamaso pace pagamukapo,Kubweza ukali wace ungawaononge,
24 Anapeputsanso dziko lofunika,Osabvomereza mau ace;
25 Koma anadandaula m'mahema mwao,Osamvera mau a Yehova.
26 Potero anawasamulira dzanja lace,Kuti awagwetse m'cipululu:
27 Kugwetsanso mbeu zao mwa amitundu,Ndi kuwabalalitsa m'maiko maiko.
28 Ndipo anadzipatikiza ndi BaalaPeori,Nadyanso nsembe za akufa.