26 Potero anawasamulira dzanja lace,Kuti awagwetse m'cipululu:
27 Kugwetsanso mbeu zao mwa amitundu,Ndi kuwabalalitsa m'maiko maiko.
28 Ndipo anadzipatikiza ndi BaalaPeori,Nadyanso nsembe za akufa.
29 Ndipo anamkwiyitsa nazo zocita zao;Kotero kuti mliri unawagwera.
30 Pamenepo panauka Pinehasi, nacita cilango:Ndi mliriwo unaletseka.
31 Ndipo adamuyesa iye wacilungamo,Ku mibadwo mibadwo ku nthawi zonse.
32 Anautsanso mkwiyo wace ku madzi a Meriba,Ndipo kudaipira Mose cifukwa ca iwowa: