28 Ndipo anadzipatikiza ndi BaalaPeori,Nadyanso nsembe za akufa.
29 Ndipo anamkwiyitsa nazo zocita zao;Kotero kuti mliri unawagwera.
30 Pamenepo panauka Pinehasi, nacita cilango:Ndi mliriwo unaletseka.
31 Ndipo adamuyesa iye wacilungamo,Ku mibadwo mibadwo ku nthawi zonse.
32 Anautsanso mkwiyo wace ku madzi a Meriba,Ndipo kudaipira Mose cifukwa ca iwowa:
33 Pakuti anawawitsa mzimu wace,Ndipo analankhula zosayenera ndi milomo yace.
34 Sanaononga mitunduyo ya anthu,Imene Mulungu adawauza;