32 Anautsanso mkwiyo wace ku madzi a Meriba,Ndipo kudaipira Mose cifukwa ca iwowa:
33 Pakuti anawawitsa mzimu wace,Ndipo analankhula zosayenera ndi milomo yace.
34 Sanaononga mitunduyo ya anthu,Imene Mulungu adawauza;
35 Koma anasokonekerana nao amitundu,Naphunzira nchito zao:
36 Ndipo anatumikira mafano ao,Amene anawakhalira msampha:
37 Ndipo anapereka ana ao amuna ndi akazi nsembe ya kwa ziwanda,
38 Nakhetsa mwazi wosacimwa, ndi wo mwazi wa ana ao amuna ndi akazi,Amene anawaperekera nsembe mafano a Kanani;M'mwemo analidetsa dziko ndi mwaziwo.