40 Potero udayaka mkwiyo wa Yehova pa anthu ace,Nanyansidwa Iye ndi colowa cace.
41 Ndipo anawapereka m'manja a amitundu;Ndipo odana nao anacita ufumu pa iwo.
42 Adani ao anawasautsanso,Nawagonjetsa agwire mwendo wao.
43 Iye anawalanditsa kawiri kawiri;Koma anapikisana ndi Iye mwa uphungu wao,Ndi mphulupulu zao zinawafoketsa,
44 Koma anapenya nsautso yao,Pakumva kupfuula kwao:
45 Ndipo anawakumbukila cipangano cace,Naleza monga mwa kucuruka kwa cifundo cace.
46 Ndipo anawacitira kuti apeze nsoniPamaso pa onse amene adawamanga ndende.