10 Ana ace akhale amcirakuyenda ndi opemphapempha;Afunefune zosowa zao kucokera m'mabwinja mwao.
11 Wokongoletsa agwire zonse ali nazo;Ndi alendo alande za nchito yace.
12 Pasakhale munthu wakumdtira cifundo;Kapena kucitira cokoma ana ace amasiye.
13 Zidzukulu zace zidulidwe;Dzina lao lifafanizidwe mu mbadwo ukudza.
14 Mphulupulu za makolo ace zikumbukike ndi Yehova;Ndi cimo la mai wace lisafafanizidwe.
15 Zikhale pamaso pa Yehova cikhalire,Kuti adule cikumbukilo cao kucicotsera ku dziko lapansi.
16 Cifukwa kuti sanakumbukila kucita cifundo,Koma analondola wozunzika ndi waumphawi,Ndi wosweka mtima, kuti awaphe.