23 Ndamuka ngati mthunzi womka m'taliNdiingidwa kwina ndi kwina ngati dzombe.
24 Mabondo anga agwedezeka cifukwa ca kusala;Ndi mnofu wanga waonda posowa mafuta.
25 Ndiwakhaliranso cotonza;Pakundiona apukusa mutu.
26 Ndithandizeni Yehova, Mulungu wanga:Ndipulumutseni monga mwa cifundo canu;
27 Kuti adziwe kuti ici ndi dzanja lanu;Kuti Inu Yehova munacicita.
28 Atemberere iwowa, koma mudalitse ndinu;Pakuuka iwowa adzacita manyazi, koma mtumiki wanu adzakondwera.
29 Otsutsana nane abvale manyazi,Nadzikute naco cisokonezo cao ngati ndi copfunda.