27 Kuti adziwe kuti ici ndi dzanja lanu;Kuti Inu Yehova munacicita.
28 Atemberere iwowa, koma mudalitse ndinu;Pakuuka iwowa adzacita manyazi, koma mtumiki wanu adzakondwera.
29 Otsutsana nane abvale manyazi,Nadzikute naco cisokonezo cao ngati ndi copfunda.
30 Ndidzayamika Yehova kwakukuru pakamwa panga;Ndi pakati pa anthu aunyinji ndidzamlemekeza.
31 Popeza adzaima pa dzanja lamanja la waumphawiKumpulumutsa kwa iwo akuweruza koipa moyo wace.