4 M'malo mwa cikondi canga andibwezera udani;Koma ine, kupemphera ndiko.
5 Ndipo anandisenza coipa m'malo mwa cokoma,Ndi udani m'malo mwa cikondi canga.
6 Muike munthu woipa akhale mkuru wace;Ndi mdani aime pa dzanja lamanja lace.
7 Ponenedwa mlandu wace aturuke wotsutsika;Ndi pemphero lace likhale ngati kucimwa.
8 Masiku ace akhale owerengeka;Wina alandire udindo wace.
9 Ana ace akhale amasiye, Ndi mkazi wace wamasiye.
10 Ana ace akhale amcirakuyenda ndi opemphapempha;Afunefune zosowa zao kucokera m'mabwinja mwao.