7 Ponenedwa mlandu wace aturuke wotsutsika;Ndi pemphero lace likhale ngati kucimwa.
8 Masiku ace akhale owerengeka;Wina alandire udindo wace.
9 Ana ace akhale amasiye, Ndi mkazi wace wamasiye.
10 Ana ace akhale amcirakuyenda ndi opemphapempha;Afunefune zosowa zao kucokera m'mabwinja mwao.
11 Wokongoletsa agwire zonse ali nazo;Ndi alendo alande za nchito yace.
12 Pasakhale munthu wakumdtira cifundo;Kapena kucitira cokoma ana ace amasiye.
13 Zidzukulu zace zidulidwe;Dzina lao lifafanizidwe mu mbadwo ukudza.