7 Yehova ndi wanga, mwa iwo akundithandiza;M'mwemo ndidzaona cofuna ine pa iwo akundida,
8 Kuthawira kwa Yehova nkokomaKoposa kukhulupirira munthu.
9 Kuthawira kwa Yehova nkokomaKoposa kukhulupirira akulu,
10 Amitundu onse adandizinga,Zedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.
11 Adandizinga, inde, adandizinga:Indedi, m'dzinala Yehova ndidzawaduladula.
12 Adandizinga ngati njuci;Anazima ngati moto waminga;Indedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.
13 Kundikankha anandikankha ndikadagwa;Koma Yehova anandithandiza.