43 Ndipo musandicotsere ndithu mau a coonadi pakamwa panga;Pakuti ndinayembekeza maweruzo anu.
44 Potero ndidzasamalira malamulo anu cisamalireKu nthawi za nthawi.
45 Ndipo ndidzayenda mwaufulu;Popeza ndinafuna malangizo anu.
46 Ndidzalankhulanso za umboni wanu pamaso pa mafumu,Osacitapo manyazi.
47 Ndipo ndidzadzikondweretsa nao malamulo anu,Amene ndiwakonda.
48 Ndidzakwezanso manja anga ku malamulo anu, amene ndiwakonda;Ndipo ndidzalingalira pa malemba anu.
49 Kumbukilani mau a kwa mtumiki wanu,Amene munandiyembekezetsa nao.