58 Ndinapemba pankhope panu ndi mtima wanga wonse:Mundicitire cifundo monga mwa mau anu.
59 Ndinaganizira njira zanga,Ndipo ndinabweza mapazi anga atsate mboni zanu.
60 Ndinafulumira, osacedwa,Kusamalira malamulo anu.
61 Anandikulunga nazo zingwe za oipa;Koma sindinaiwala cilamulo canu.
62 Pakati pa usiku ndidzauka kukuyamikaniCifukwa ca maweruzo anu olungama.
63 Ine ndine wakuyanjana nao onse akukuopani,Ndi iwo akusamalira malangizo anu.
64 Dziko lapansi lidzala naco cifundo canu, Yehova;Mundiphunzitse malemba anu.