86 Malamulo anu onse ngokhulupirika;Andilondola nalo bodza; ndithandizeni.
87 Akadandithera pa dziko lapansi; Koma ine sindinasiya malangizo anu.
88 Mundipatse moyo monga mwa cifundo canu;Ndipo ndidzasamalira mboni ya pakamwa panu,
89 Mau anu aikika kumwamba,Kosatha, Yehova.
90 Cikhulupiriko canu cifikira mibadwo mibadwo;Munakhazikitsa dziko lapansi, ndipo likhalitsa.
91 Kunena za maweruzo anu alimbikira kufikira lero;Pakuti onsewa ndiwo atumiki anu.
92 Cilamulo canu cikadapanda kukhala cikondweretso canga,Ndikadatayika m'kuzunzika kwanga.