1 Haleluya;Lemekezani dzina la Yehova;Lemekezani inu atumiki a Yehova:
2 Inu akuimirira m'nyumba ya Yehova,M'mabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Lemekezani Yehova; pakuti Yehova ndiye wabwino;Muyimbire zolemekeza dzina lace; pakuti nkokondweretsa kutero.
4 Pakuti Yehova anadzisankhira Yakobo,Israyeli, akhale cuma cace ceni ceni.