11 Sihoni mfumu ya Aamori,Ndi Ogi mfumu ya Basana,Ndi maufumu onse a Kanani:
12 Ndipo anapereka dziko lao likhale cosiyira,Cosiyira ca kwa Israyeli anthu ace.
13 Dzina lanu, Yehova, likhala kosatha;Cikumbukilo canu, Yehova, kufikira mibadwo mibadwo.
14 Pakuti Yehova adzaweruza anthu ace,Koma adzaleka atumiki ace.
15 Mafano a amitundu ndiwo siliva ndi golidi,Nchito ya manja a anthu.
16 Pakamwa ali napo koma osalankhula;Maso ali nao, koma osapenya;
17 Makutu ali nao, koma osamva;Inde, pakamwa pao palibe mpweya.