1 Yamikani Yehova pakuti ndiye wabwino:Pakuti cifundo cace ncosatha.
2 Yamikani Mulungu wa milungu:Pakuti cifundo cace ncosatha.
3 Yamikani Mbuye wa ambuye:Pakuti cifundo cace ncosatha.
4 Amene yekha acita zodabwiza zazikuru:Pakuti cifundo cace ncosatha.
5 Amene analenga zakumwamba mwanzeru:Pakuti cifundo cace ncosatha.
6 Amene anayala dziko lapansi pamwamba pa madzi:Pakuti cifundo cace ncosatha.
7 Amene analenga miuni yaikuru:Pakuti cifundo cace ncosatha.