4 Pakuti asanafike mau pa lilime langa,Taonani, Yehova, muwadziwa onse.
5 Munandizinga kumbuyo ndi kumaso,Nimunaika dzanja lanu pa ine.
6 Kudziwa ici kundilaka ndi kundidabwiza:Kundikhalira patali, sindifikirako.
7 Ndidzapita kuti kuzembera mzimu wanu?Kapena ndidzathawira kuti kuzembera nkhope yanu?
8 Ndikakwera kumka kumwamba, muli komweko;Kapena ndikadziyalira ku Gehena, taonani, muli komweko.
9 Ndikadzitengera mapiko a mbanda kuca,Ndi kukhala ku malekezero a nyanja;
10 Kungakhale komweko dzanja lanu lidzanditsogolera,Nilidzandigwira dzanja lanu lamanja.