1 Yehova, ndaitana kwa Inu; ndifulumireni ine;Mundicherere khutu, pamene ndiitana kwa Inu.
2 Pempherolanga liikike ngaticofukiza pamaso panu;Kukweza manja anga kuikike ngati nsembe ya madzulo.
3 Muike mdindo pakamwa panga, Yehova;Sungani pakhomo pa milomo yanga.
4 Mtima wanga usalinge ku cinthu coipa,Kucita nchito zoipaNdi anthu akucita zopanda pace;Ndipo ndisadye zankhuli zao.