3 Yehova, munthu ndani kuti mumdziwa?Mwana wa munthu kuti mumsamalira?
4 Munthu akunga mpweya;Masiku ace akunga mthunzi wopitirira.
5 Weramutsani thambo lanu, Yehova, nimutsike:Khudzani mapiri ndipo adzafuka.
6 Ng'animitsani mphezi, ndi kuwabalalitsa;Tumizani mibvi yanu, ndi kuwapitikitsa,
7 Turutsani manja anu kucokera m'mwamba;Ndikwatuleni ndi kundilanditsa ku madzi akuru,Ku dzanja la alendo;
8 Amene pakamwa pao alankhula zacabe,Ndi dzanja lao lamanja ndilo dzanja lacinyengo.
9 Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano, Mulungu;Pa cisakasa ca zingwe khumi ndidzayimbira zakukulemekezani.