10 Nchito zanu zonse zidzakuyamikani, Yehova;Ndi okondedwa anu adzakulemekezani.
11 Adzanenera ulemerero wa ufumu wanu,Adzalankhulira mphamvu yanu;
12 Kudziwitsa ana a anthu zamphamvu zace,Ndi ulemerero waukuru wa ufumu wace.
13 Ufumu wanu ndiwo ufumu womka muyaya,Ndi kuweruza kwanu kufikira mibadwo yonse yonse.
14 Yehova agwiriziza onse akugwa,Naongoletsa onse owerama.
15 Maso a onse ayembekeza Inu;Ndipo muwapatsa cakudya cao m'nyengo zao.
16 Muniowetsa dzanja lanu,Nimukwaniritsira zamoyo zonse cokhumba cao.