7 Adzabukitsa cikumbukilo ca ubwino wanu waukuru,Nadzayimbira cilungamo canu.
8 Yehova ndiye wacisomo, ndi wacifundo;Osakwiya msanga, ndi wa cifundo cacikuru.
9 Yehova acitira cokoma onse;Ndi nsoni zokoma zace zigwera nchito zace zonse.
10 Nchito zanu zonse zidzakuyamikani, Yehova;Ndi okondedwa anu adzakulemekezani.
11 Adzanenera ulemerero wa ufumu wanu,Adzalankhulira mphamvu yanu;
12 Kudziwitsa ana a anthu zamphamvu zace,Ndi ulemerero waukuru wa ufumu wace.
13 Ufumu wanu ndiwo ufumu womka muyaya,Ndi kuweruza kwanu kufikira mibadwo yonse yonse.