4 Awerenga nyenyezi momwe ziri;Azicha maina zonsezi.
5 Ambuye wathu ndi wamkuru ndi wa mphamvu zambiri;Nzeru yace njosatha.
6 Yehova agwiriziza ofatsa;Atsitsira oipa pansi.
7 Yamikani Yehova ndi kuthira mang'ombe;Myimbireni Mulungu wathu zamlemekeza pazeze:
8 Amene aphimba thambo ndi mitambo,Amene akonzera mvula nthaka,Amene aphukitsa msipu pamapiri.
9 Amene apatsa zoweta cakudya cao,Ana a khungubwi alikulira.
10 Mphamvu ya kavalo siimkonda:Sakondwera nayo miyendo ya munthu.