15 Ndipo zidaoneka zoyendamo madzi,Nafukuka maziko a dziko lapansi,Mwa kudzudzula kwanu, Yehova,Mwa mpumo wa mpweya wa m'mphuno mwanu.
16 Anatuma kucokera m'mwamba, ananditenga;Anandibvuula m'madzi ambiri.
17 Anandipulumutsa ine kwa mdani wanga wamphamvu,Ndi kwa iwo ondida ine, pakuti anandiposa mphamvu.
18 Anandipeza ine tsiku la tsoka langa;Koma Yehova anali mcirikizo wanga.
19 Ananditurutsanso andifikitse motakasuka;Anandilanditsa, pakuti anakondwera ndi ine.
20 Yehova anandibwezera monga mwa cilungamo canga;Anandisudzula monga mwa kusisira kwa manja anga.
21 Pakuti ndasunga njira za Yehova,Ndipo sindinacitira coipa kusiyana ndi Mulungu wanga.