23 Ndipo ndinakhala wangwiro ndi iye,Ndipo ndinadzisunga wosacita coipa canga.
24 Ndimo anandisudzulira Yehova monga mwa cilungamo canga,Monga mwa kusisira kwa manja anga pamaso pace.
25 Pa wacifundo mukhala wacifundoPa mumthu wangwiro mukhala wangwiro;
26 Pa woyera mtima mukhala woyera mtima;Pa wotsutsatsutsa mukhala wotsutsana naye.
27 Pakuti Inu muwapulumutsa anthu aumphawi;Koma maso okweza muwatsitsa.
28 Pakuti Inu muyatsa nyali yanga;Yehova, Mulungu wanga, aunikira mdima wanga.
29 Pakuti mwa Inu ndipyola khamu la anthu;Ndipo mwa Mulungu wanga ndilumphira linga.