26 Pa woyera mtima mukhala woyera mtima;Pa wotsutsatsutsa mukhala wotsutsana naye.
27 Pakuti Inu muwapulumutsa anthu aumphawi;Koma maso okweza muwatsitsa.
28 Pakuti Inu muyatsa nyali yanga;Yehova, Mulungu wanga, aunikira mdima wanga.
29 Pakuti mwa Inu ndipyola khamu la anthu;Ndipo mwa Mulungu wanga ndilumphira linga.
30 Mulungu ndiyewangwiro m'njira zace;Mau a Yehova ngoyengeka; Ndiye cikopa ca onse okhulupirira Iye.
31 Pakuti Mulungu ndani wosati Yehova?Ndipo thanthwe ndani wosati Mulungu wathu?
32 Mulungu ndiye wondizingiza mphamvu m'cuuno,Nakonza njira yanga ikhale yangwiro.